Unknown

Unknown - Malawi Native Anthem Text lyrics

rate me

1.

Mlungu dalitsani Malawi,

Mumsunge m'mtendere.

Gonjetsani adani onse,

Njala, nthenda, nsanje.

Lunzitsani mitima yathu,

Kuti tisaope.

Mdalitse Mtsogo leri na fe,

Ndi Mai Malawi.

2.

Malawi ndziko lokongola,

La chonde ndi ufulu,

Nyanja ndi mphepo ya m'mapiri,

Ndithudi tadala.

Zigwa, mapiri, nthaka, dzinthu,

N'mphatso zaulere.

Nkhalango, madambo abwino.

Ngwokoma Malawi.

3.

O! Ufulu tigwirizane,

Kukweza Malawi.

Ndi chikondi, khama, kumvera,

Timutumikire.

Pa nkhondo nkana pa mtendere,

Cholinga n'chimodzi.

Mai, bambo, tidzipereke,

Pokweza Malawi.

Sent by Carlos André Pereira da Silva Branco

Get this song at:  amazon.com  sheetmusicplus.com

Share your thoughts

0 Comments found