Maskal

Maskal - Ndiwe Wanga lyrics

rate me

<b>Ndiwe Wanga</b> by <i>Maskal</i><br />

Verse; 1

Pazachikondi chako dziwa ine ndi mboni

Sindinalakelake kupita ku Joni

Chikondi cha iwe ndi ine sicham'mafoni

Nchifukwa sindinapite ku bank kukatenga loan

Chikondi chathu chobeba chanoninoni

Umandizula moyo ukapereka moni

Umandikumbutsa za kwathu kumangoni

Ndakondwa umadziwa kuti ine ndi m'goni

Chorus*2

Ndiwe wanga ndiwe kuwala kwanga

Ndiwe wanga ndiwe nyenyezi yanga

Ndiwe wanga ndiwe wanga ndiwe wapamtima wanga

Ndiwe wanga ndiwe wanga nyenyezi yanga

Ndiwe wanga ndiwe kuwala kwanga

Verse; 2

Ndikakha pansi ndimadziwa ndiri ndi mzanga

Kuyenda limodzi tifanana mawanga

Amandinena ati ndiri nyanga

Asatilongoze monga ichita nkhanga

Ndithudi ndilonjeza ndzakutengela kunyanja

Nthawi imeneyo tikukonzekera banja

Ona ambiri akutiombera m'manja

Mpakana wena kutimangira nsanja

(Back to chorus)

Verse; 3

Chikondi chathu chansangala sizachisoni

Ena amasangalala akatipatsa moni

Unasiya amabenzi onse ndimalinkoni

Amatithila madzi ndikumaimba horn

Akamaditsa baby, Samamvetsa baby

Ngati andale baby, Ali pa njale baby

Zimawawawa baby, Kuiwala mawa baby

Ngati moyenda baby, Ife tikuyenda baby!, Hee!

(Back to chorus till the end)

Get this song at:  amazon.com  sheetmusicplus.com

Share your thoughts

0 Comments found